Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 35:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Mose anasonkhanitsa khamu lonse la ana a Israyeli, nanena nao, Siwa mau amene Yehova anauza, kuti muwacite.

2. Masiku asanu ndi limodzi azigwira nchito; koma tsiku lacisanu ndi ciwiri muliyese lopatulika, Sabata lakupuma la Yehova: ali yense agwira nchito pamenepo, aphedwe,

3. Musamasonkha mota m'nyumba zanu ziri zonse tsiku la Sabata.

4. Ndipo Mose ananena ndi khamu lonse la ana a Israyeli, ndi kuti, Ici ndi cimene Yehova anauza ndi kuti,

5. Mumtengere Yehova copereka ca mwa zanu; ali yense wa mtima womfunitsa mwini abwere naco, ndico copereka ca Yehova;

6. golidi, ndi siliva, ndi mkuwa; ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi;

7. ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wasitimu;

8. ndi mafuta akuunikira, ndi zonunkhira za mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma;

9. ndi miyala yasohamu, ndi miyala yoika ya efodi, ndi ya capacifuwa.

10. Ndipo abwere yense wa mtima waluso mwa inu, napange zonse zimene Yehova anauza;

11. kacisi, hema wace, ndi cophimba cace, zokowera zace, ndi matabwa ace, mitanda yace, mizati, nsanamira, ndi nsici zace, ndi makamwa ao;

12. likasa, ndi mphiko zace, cotetezerapo, ndi nsaru yocinga yotseka;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 35