33. Ndipo Yehova anati kwa Mose, iye amene wandicimwira, ndifafaniza yemweyo kumcotsa m'buku langa.
34. Ndipo tsopano, muka, tsogolera anthu kumka nao kumene ndinakuuza; taona, mthenga wanga akutsogolera; koma tsiku lakuwazonda Ine ndidzawalanga cifukwa ca kucimwa kwao.
35. Ndipo Yehova anakantha anthu, cifukwa anapanga mwana wa ng'ombe amene Aroni anapanga.