Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 31:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. ndipo ndamdzaza nd mzimu wa Mulungu, ndi luso, ndi nzeru, ndi cidziwitso, ndi m'nchito ziri zonse,

4. kulingirira nchito zaluso, kucita ndi golidi ndi siliva ndi mkuwa,

5. ndi kuzokota miyala yoikika, ndi kuzokota mtengo, kucita nchito ziri zonse.

6. Ndipo Ine, taona, ndampatsa Aholiabu, mwana wa Ahisama, wa pfuko la Dani, akhale naye; ndipo ndaika luso m'mitima ya onse a mtima waluso, kuti apange zonse ndakuuza iwe;

7. cihema cokomanako, likasa la mboni, ndi cotetezerapo ciri pamwamba pace, ndi zipangizo zonse za cihemaco;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 31