34. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Udzitengere zonunkhira, natafi, ndi sekeleti, ndi kelebuna; zonunkhira pamodzi ndi libano loona; miyeso yofanana;
35. ndipo uzikonza nazo cofukiza, cosanganiza mwa macitidwe a wosanganiza, cokometsera ndi mcere, coona, copatulika;
36. nupere cina cisalale, nuciike cakuno ca mboni m'cihema cokomanako, kumene ndidzakomana ndi iwe; uciyese copatulika ndithu.
37. Koma za cofukizaco ucikonze, musadzikonzere nokha cina, mwa makonzedwe ace amene; muciyese copatulika ca Yehova.
38. Ali yense wokonza cina cotere kununkhizapo, asadzidwe kwa anthu a mtundu wace.