24. ndi kida mazana asanu, monga sekeli la malo opatulika, ndi mafuta a azitona hini limodzi;
25. ndipo ukonze nazo mafuta odzoza opatulika, osanganizika monga mwa macitidwe a wosanganiza; akhale mafuta odzoza opatulika.
26. Ndipo udzoze nao cihema cokomanako, ndi likasa la mboni,
27. ndi gomelo ndi zipangizo zace zonse, ndi coikapo nyali ndi zipangizo zace,