Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 30:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo Aroni ndi ana ace amuna azisambiramo manja ao ndi mapazi ao;

20. pakulowa iwo m'cihema cokomanako asambe ndi madzi, kuti angafe; kapena poyandikiza guwa la nsembe kutumikirako, kufukiza nsembe yamoto ya Yehova;

21. asambe manja ao ndi mapazi ao, kuti angafe: liwakhalire lemba losatha, kwa iye ndi kwa mbeu zace, mwa mibadwo yao.

22. Yehova ananenanso ndi Mose, ndi kuti,

23. Udzitengerenso zonunkhira zomveka, mure woyenda masekeli mazana asanu, ndi kinimani lonunkhira limodzi mwa magawo awiri a mureyo, ndilo masekeli mazana awiri kudza makumi asanu, ndi kane lonunkhira mazana awiri kudza makumi asanu,

Werengani mutu wathunthu Eksodo 30