Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 30:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Yense wakupita kwa owerengedwawo, wa zaka makumi awiri ndi wa mphambu zace, apereke coperekaco kwa Yehova.

15. Wacuma asacurukitsepo, ndi osauka asacepse pa limodzi mwa magawo awiri a sekeli, pakupereka copereka kwa Yehova, kucita coteteza ca miyoyo yanu.

16. Ndipo uzilandira ndarama za coteteza kwa ana a Israyeli, ndi kuzipereka pa nchito ya cihema cokomanako; kuti zikhale cikumbutso ca ana a Israyeli pamaso pa Yehova, kucita coteteza ca miyoyo yanu.

17. Ndipo Yehova analankhula ndi Mose, ndi kuti,

18. Upangenso mkhate wamkuwa, ndi tsinde lace lamkuwa, wakusambiramo; nuuike pakati pa ciliema cokomanako ndi guwa la nsembe, ndi kuthiramo madzi.

19. Ndipo Aroni ndi ana ace amuna azisambiramo manja ao ndi mapazi ao;

20. pakulowa iwo m'cihema cokomanako asambe ndi madzi, kuti angafe; kapena poyandikiza guwa la nsembe kutumikirako, kufukiza nsembe yamoto ya Yehova;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 30