Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 29:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ici ndico uwacitire kuwapatula, andicitire nchito ya nsembe: tenga ng'ombe yamphongo, ndi nkhosa ziwiri zamphongo zangwiro,

2. ndi mkate wopanda cotupitsa, ndi timitanda topanda cotupitsa tosanganiza ndi mafuta, ndi timitanda taphanthi topanda cotupitsa, todzoza ndi mafuta; utipange ndi ufa wosalala watirigu.

3. Ndipo uziike mu mtanga umodzi, ndi kubwera nazo mumtanga, pamodzi ndi ng'ombe yamphongo ndi nkhosa ziwiri zamphongo.

4. Ndipo ubwere nao Aroni ndi ana ace amuna ku khomo la cihema cokomanako indi kuwasambitsa m'madzi.

5. Pamenepo utenge zobvalazo ndi kubveka Aroni maraya am'kati, ndi mwinjiro wa efodi, ndi efodi, ndi capacifuwa, ndi kummangira m'cuuno ndi mpango wa efodi woluka mwanzeru;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 29