Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 25:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2. Lankhula ndi ana a Israyeli, kuti anditengere copereka; ulandire copereka canga kwa munthu ali yense mtima wace umfunitsa mwini.

3. Ndipo coperekaco ucilandire kwa iwo ndi ici: golidi, ndi, siliva, ndi mkuwa,

4. ndi lamadzi, ndi: lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi;

5. ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wasitimu;

6. mafuta akuunikira, zonunkhira za mafuta odzoza, ndi za cofukiza ca pfungo lokoma;

7. miyala yaberulo, ndi miyala yoika paefodi, ndi pacapacifuwa.

8. Ndipo andimangire malo opatulika; kuti ndikhale pakati pao,

9. Monga mwa zonse Ine ndirikuonetsa iwe, cifaniziro ca kacisi, ndi cifaniziro ca zipangizo zace zonse, momwemo ucimange.

10. Ndipo azipanga likasa la mtengo wasitimu: utali wace mikono iwiri ndi hafu, kupingasa kwace mkono ndi hafu, msinkhu wace mkono ndi hafu.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 25