Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 23:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Usatola mbiri yopanda pace; usathandizana naye woipa ndi kukhala mboni yocititsa ciwawa.

2. Usatsata unyinji wa anthu kucita coipa; kapena usacita umboni kumlandu, ndi kupatukira kutsata unyinji ndi kukhotetsa mlandu;

3. kapena usakometsera munthu wosauka pa mlandu wace.

4. Ukakomana ndi ng'ombe kapena buru wa mdani wako zirimkusokera, uzimbwezera izo ndithu.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 23