Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 22:21-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo usasautsa mlendo kapena kumpsinja; pakuti munali alendo m'dziko la Aigupto.

22. Musazunza mkazi wamasiye, kapena mwana wamasiye ali yense.

23. Ukawazunza ndi kakuti konse, nakandilirira pang'ono ponse iwowa, ndidzamvadi kulira kwao;

24. ndi mkwiyo wanga idzayaka, ndipo ndidzapha inu ndi lupanga; ndipo akazi anu adzakhala amasiye, ndi ana anu omwe.

25. Ukakongoletsa ndalama anthu anga osauka okhala nanu, usamkhalira ngati wangongole; usamwerengera phindu.

26. Ukati ulandire cikole kaya cobvala ca mnansi wako, koma polowa dzuwa ucibwezere kwa iye;

27. popeza copfunda cace ndi ici cokha, ndico cobvala ca pathupi pace; azipfundira ciani pogona? Ndipo kudzakhala kuti akandipfuulira Ine, ndidzamva; pakuti Ine ndine wacisomo.

28. Usapeputsa oweruza, kapena kutemberera mkuru wa anthu a mtundu wako.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 22