Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 22:17-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Atate wace akakana konse kumpatsa iye, alipe ndalama monga mwa colipa ca anamwali.

18. Wanyanga usamlola akhale ndi moyo.

19. Ali yense agona ndi coweta aphedwe ndithu.

20. Wakuphera nsembe mulungu wina, wosati Yehova yekha, aonongeke konse.

21. Ndipo usasautsa mlendo kapena kumpsinja; pakuti munali alendo m'dziko la Aigupto.

22. Musazunza mkazi wamasiye, kapena mwana wamasiye ali yense.

23. Ukawazunza ndi kakuti konse, nakandilirira pang'ono ponse iwowa, ndidzamvadi kulira kwao;

24. ndi mkwiyo wanga idzayaka, ndipo ndidzapha inu ndi lupanga; ndipo akazi anu adzakhala amasiye, ndi ana anu omwe.

25. Ukakongoletsa ndalama anthu anga osauka okhala nanu, usamkhalira ngati wangongole; usamwerengera phindu.

26. Ukati ulandire cikole kaya cobvala ca mnansi wako, koma polowa dzuwa ucibwezere kwa iye;

27. popeza copfunda cace ndi ici cokha, ndico cobvala ca pathupi pace; azipfundira ciani pogona? Ndipo kudzakhala kuti akandipfuulira Ine, ndidzamva; pakuti Ine ndine wacisomo.

28. Usapeputsa oweruza, kapena kutemberera mkuru wa anthu a mtundu wako.

29. Usacedwa kuperekako zipatso zako zocuruka, ndi zothira zako. Woyamba wa ana ako amuna undipatse Ine.

30. Uzitero nazo ng'ombe zako, ndi nkhosa zako; masiku asanu ndi atatu akhale ndi amai wace; tsiku lacisanu ndi citatu uzimpereka kwa Ine.

31. Ndipo muzindikhalira Ine anthu opatulika; cifukwa cace musamadya nyama yojiwa kuthengo; itayireni agaru.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 22