Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 22:13-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ngati cajiwa ndithu, abwere naco cikhale mboni; asalipe pa cojiwaco.

14. Munthu akabwereka cinthu kwa mnansi wace, ndipo ciphwetekwa, kapena cifa, mwiniyo palibe, azilipa ndithu.

15. Akakhalapo mwiniyo, asalipe; ngati cagwirira nchito yakulipira, cadzera kulipira kwace.

16. Munthu akanyenga namwali wosapalidwa ubwenzi, nakagona nave, alipetu kuti akhale mkazi wace.

17. Atate wace akakana konse kumpatsa iye, alipe ndalama monga mwa colipa ca anamwali.

18. Wanyanga usamlola akhale ndi moyo.

19. Ali yense agona ndi coweta aphedwe ndithu.

20. Wakuphera nsembe mulungu wina, wosati Yehova yekha, aonongeke konse.

21. Ndipo usasautsa mlendo kapena kumpsinja; pakuti munali alendo m'dziko la Aigupto.

22. Musazunza mkazi wamasiye, kapena mwana wamasiye ali yense.

23. Ukawazunza ndi kakuti konse, nakandilirira pang'ono ponse iwowa, ndidzamvadi kulira kwao;

24. ndi mkwiyo wanga idzayaka, ndipo ndidzapha inu ndi lupanga; ndipo akazi anu adzakhala amasiye, ndi ana anu omwe.

25. Ukakongoletsa ndalama anthu anga osauka okhala nanu, usamkhalira ngati wangongole; usamwerengera phindu.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 22