Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 22:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ngati cajiwa ndithu, abwere naco cikhale mboni; asalipe pa cojiwaco.

14. Munthu akabwereka cinthu kwa mnansi wace, ndipo ciphwetekwa, kapena cifa, mwiniyo palibe, azilipa ndithu.

15. Akakhalapo mwiniyo, asalipe; ngati cagwirira nchito yakulipira, cadzera kulipira kwace.

16. Munthu akanyenga namwali wosapalidwa ubwenzi, nakagona nave, alipetu kuti akhale mkazi wace.

17. Atate wace akakana konse kumpatsa iye, alipe ndalama monga mwa colipa ca anamwali.

18. Wanyanga usamlola akhale ndi moyo.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 22