Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 22:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Koma ngati cidabedwa kwaoko ndithu, alipe kwa mwiniyo.

13. Ngati cajiwa ndithu, abwere naco cikhale mboni; asalipe pa cojiwaco.

14. Munthu akabwereka cinthu kwa mnansi wace, ndipo ciphwetekwa, kapena cifa, mwiniyo palibe, azilipa ndithu.

15. Akakhalapo mwiniyo, asalipe; ngati cagwirira nchito yakulipira, cadzera kulipira kwace.

16. Munthu akanyenga namwali wosapalidwa ubwenzi, nakagona nave, alipetu kuti akhale mkazi wace.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 22