12. Koma ngati cidabedwa kwaoko ndithu, alipe kwa mwiniyo.
13. Ngati cajiwa ndithu, abwere naco cikhale mboni; asalipe pa cojiwaco.
14. Munthu akabwereka cinthu kwa mnansi wace, ndipo ciphwetekwa, kapena cifa, mwiniyo palibe, azilipa ndithu.
15. Akakhalapo mwiniyo, asalipe; ngati cagwirira nchito yakulipira, cadzera kulipira kwace.
16. Munthu akanyenga namwali wosapalidwa ubwenzi, nakagona nave, alipetu kuti akhale mkazi wace.