Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 22:11-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. lumbiro la Yehova likhale pakati pa iwo awiri, kuti sanaturutsa dzanja lace pa cuma ca mnansi wace; ndipo mwiniyo azibvomereza, ndipo asalipe.

12. Koma ngati cidabedwa kwaoko ndithu, alipe kwa mwiniyo.

13. Ngati cajiwa ndithu, abwere naco cikhale mboni; asalipe pa cojiwaco.

14. Munthu akabwereka cinthu kwa mnansi wace, ndipo ciphwetekwa, kapena cifa, mwiniyo palibe, azilipa ndithu.

15. Akakhalapo mwiniyo, asalipe; ngati cagwirira nchito yakulipira, cadzera kulipira kwace.

16. Munthu akanyenga namwali wosapalidwa ubwenzi, nakagona nave, alipetu kuti akhale mkazi wace.

17. Atate wace akakana konse kumpatsa iye, alipe ndalama monga mwa colipa ca anamwali.

18. Wanyanga usamlola akhale ndi moyo.

19. Ali yense agona ndi coweta aphedwe ndithu.

20. Wakuphera nsembe mulungu wina, wosati Yehova yekha, aonongeke konse.

21. Ndipo usasautsa mlendo kapena kumpsinja; pakuti munali alendo m'dziko la Aigupto.

22. Musazunza mkazi wamasiye, kapena mwana wamasiye ali yense.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 22