Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 20:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Mulungu ananena mau onse amenewa, nati:

2. INE ndine YEHOVA Mulungu wako, amene ndinaturutsa iwe ku dziko la Aigupto, ku nyumba ya akapolo.

3. Usakhale nayo milungu yina koma Ine ndekha.

4. Usadzipangire iwe wekha fano losema, kapena cifaniziro ciri conse ca zinthu za m'thambo la kumwamba, kapena za m'dziko lapansi, kapena za m'madzi a pansi pa dziko;

5. usazipembedzere izo, usazitumikire izo; cifukwa Ine Yehova Mulungu wako ndiri Mulungu wansanje, wakulanga ana cifukwa ca atate ao, kufikira mbadwo wacitatu ndi wacinai wa iwo amene akudana ndi Ine;

6. ndi kuwacitira cifundo anthu zikwizikwi a iwo amene akondana ndi Ine, nasunga malamulo anga.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 20