Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 16:32-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Ndipo Mose anati, Awa ndi mau anauza Yehova, Dzazani omeri nao, asungikire mibadwo yanu; kuti aone mkatewo ndinakudyetsani nao m'cipululu, muja ndinakuturutsani m'dziko la Aigupto.

33. Ndipo Mose anati kwa Aroni, Tenga mphika, nuthiremo mana odzala omeri, nuuike pamaso pa Yehova, usungikire mibadwo yanu.

34. Monga Yehova anauza Mose, momwemo Aroni anauika patsogolo pa Mboni, usungikeko.

35. Ndipo ana a Israyeli anadya mana zaka makumi anai, kufikira atalowa dziko la midzi; anadya mana kufikira analowa malire a dziko la Kanani.

36. Koma omeri ndilo limodzi la magawo khumi la efa.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 16