Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 16:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Amenewo ndiwo mau walamulira Yehova, Aoleko yense monga mwa njala yace; munthu mmodzi omeri limodzi, monga momwe muli, yense atengere iwo m'hema mwace.

17. Ndipo ana a Israyeli anatero, naola wina wambiri, wina pang'ono.

18. Ndipo pamene anayesa ndi omeri, iye amene adaola wambiri sunamtsalira, ndi iye amene adaola pang'ono sunamsowa; yense anaola monga mwa njala yace.

19. Ndipo Mose ananena nao, Palibe munthu asiyeko kufikira m'mawa.

20. Koma sanammvera Mose; ndipo ena anasiyako kufikira m'mawa; koma unagwa mphutsi, nununkha. Ndipo Mose anakwiya nao.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 16