Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 15:6-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Dzanja lanu lamanja, Yehova, lalemekezedwa ndi mphamvu,Dzanja lanu lamanja, Yehova, laphwanya mdani.

7. Ndipo ndi ukulu wanu waukuru mwapasula akuukira Inu;Mwatumiza mkwiyo wanu, unawanyeketsa ngati ciputu.

8. Ndipondi mpumo wa m'mphuno mwanu madzi anaunjikika,Mayendedwe ace anakhala ciriri ngati mulu;Zozama zinalimba m'kati mwa nyanja.

9. Mdani anati,Ndiwalondola, ndiwakumika, ndidzagawa zofunkha;Ndidzakhuta nao mtima;Ndidzasolola lupanga langa, dzanja langa lidzawaononga.

10. Munaombetsa mphepo yanu, nyanja inawamiza;Anamira m'madzi akuru ngati mtobvu.

11. Manana ndi Inu ndani mwa milungu, Yehova?Manana ndi Inu ndani, wolemekezedwa, woyera,Woopsa pomyamika, wakucita zozizwa?

12. Mwatambasula dzanja lanu lamanja,Nthaka inawameza,

Werengani mutu wathunthu Eksodo 15