Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 12:46-51 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

46. Audye m'nyumba imodzi; usaturukira nayo kubwalo nyama yina; ndipo musathyole pfupa lace.

47. Msonkhano wonse wa Israyeli uzicita ici.

48. Koma akakhala nanu mlendo, nakonzera Yehova Paskha, adulidwe amuna ace onse, ndipo pamenepo asendere kuucita; nakhale ngati wobadwa m'dziko; koma wosadulidwa ali yense asadyeko.

49. Pakhale lamulo lomweli pa wobadwa m'dziko, ndi pa mlendo wakukhala pakati pa inu.

50. Ndipo ana onse a Israyeli anacita monga Yehova adawalamulira Mose ndi Aroni, momwemo anacita.

51. Ndipo kunakhala tsiku lomwelo, kuti Yehova anaturutsa ana a Israyeli m'dziko la Aigupto, monga mwa makamu ao.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 12