14. Musamatsata milungu yina, milungu yina ya mitundu ya anthu akuzinga inu;
15. pakuti Yehova Mulungu wanu ali pakati panu, ndiye Mulungu wansanje; kuti ungapse mtima wa Yehova Mulungu wanu, ndi kukuonongani, kukucotsani pankhope pa dziko lapansi.
16. Musamayesa Yehova Mulungu wanu, monga munamyesa m'Masa.
17. Muzisunga mwacangu malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi mboni zace, ndi malemba ace, amene anakulamulirani.
18. Ndipo muzicita zolunjika ndi zokoma pamaso pa Yehova; kuti cikukomereni, ndi kuti mulowe kukalandira dziko lokomali Yehova analumbirira makolo anu,