Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 5:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakuturutsa m'dziko la Aigupto, m'nyumba ya akapolo.

7. Usakhale nayo milungu yina koma Ine ndekha.

8. Usadzipangire iwe wekha fano losema, kapena cifaniziro ciri conse ca zinthu za m'thambo la kumwamba, kapena za m'dziko lapansi, kapena za m'madzi a pansi pa dziko;

9. usazipembedzere izo, usazitumikire izo; cifukwa Ine Yehova Mulungu wako ndine Mulungu wansanje, wakulanga ana cifukwa ca atate wao, kufikira mbadwo wacitatu ndi wacinai wa iwo amene akudana ndi Ine;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 5