Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 5:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Mose anaitana Israyeli wonse, nanena nao, Tamverani, Israyeli, malemba ndi maweruzo ndinenawa m'makutu mwanu lero, kuti muwaphunzire, ndi kusamalira kuwacita.

2. Yehova Mulungu wathu anapangana nafe cipangano m'Horebe.

3. Yehova sanacita cipangano ici ndi makolo athu, koma ndi ife, ife amene tiri ndi moyo tonsefe pane lero.

4. Yehova ananena ndi inu popenyana maso m'phirimo, ali pakati pa moto,

5. (ndinalinkufma pakati pa Yehova ndi inu muja, kukulalikirani mau a Yehova; popeza munacita mantha cifukwa ca moto, osakwera m'phirimo) ndi kuti:

6. Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakuturutsa m'dziko la Aigupto, m'nyumba ya akapolo.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 5