Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 5:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Mose anaitana Israyeli wonse, nanena nao, Tamverani, Israyeli, malemba ndi maweruzo ndinenawa m'makutu mwanu lero, kuti muwaphunzire, ndi kusamalira kuwacita.

2. Yehova Mulungu wathu anapangana nafe cipangano m'Horebe.

3. Yehova sanacita cipangano ici ndi makolo athu, koma ndi ife, ife amene tiri ndi moyo tonsefe pane lero.

4. Yehova ananena ndi inu popenyana maso m'phirimo, ali pakati pa moto,

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 5