Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 32:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Kumbukirani masiku akale,Zindikirani zaka za mibadwo yambiri;Funsani atate wanu, adzakufotokozerani;Akuru anu, adzakuuzani.

8. Pamene Wam'mwambamwamba anagawira amitundu colowacao,Pamene anagawa ana a anthu,Anaika malire a mitundu ya anthu,Monga mwa kuwerenga kwao kwa ana a Israyeli,

9. Pakuti gawo la Yehova ndilo anthu ace;Yakobo ndiye muyeso wa colowacace.

10. Anampeza m'dziko la mabwinja, ndi m'cipululu colira copanda kanthu;Anamzinga, anamlangiza,Anamsunga ngati kamwana lea m'diso;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 32