48. Ndipo Yehova ananena ndi Mose tsiku lomweli, ndi kuti,
49. Kwera m'phiri muno mwa Abarimu, phiri la Nebo, lokhala m'dziko la Moabu, popenyana ndi Yeriko; nupenye dziko la Kanani, limene ndipereka kwa ana a Israyeli likhale lao lao;
50. nufe m'phiri m'mene ukweramo, nuitanidwe kumka kwa anthu a mtundu wako; monga Aroni mbale wako anafa m'phiri la Hori, naitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wace;
51. popeza munandilakwira pakati pa ana a Israyeli ku madzi a Meriba wa Kadesi m'cipululu ca Zini, popeza simunandipatula Ine pakati pa ana a Israyeli,
52. Pakuti udzapenya dzikoli pandunji pako; koma osalowako ku dziko limene ndipatsa ana a Israyeli.