Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 32:23-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndidzawaunjikira zoipa;Ndidzawathera nubvi yanga.

24. Adzaonda nayo njalaAdzanyekeka ndi makala a moto, cionongeko cowawa;Ndipo ndidzawatumizira mana a zirombo,Ndi ululu wa zokwawa m'pfumbi.

25. Pabwalo lupanga lidzalanda,Ndi m'zipinda mantha;Lidzaononga mnyamata ndi namwali,Woyamwa pamodzi ndi munthu waimvi.

26. Ndinati, Ndikadawauzira ndithu,Ndikadafafaniza cikumbukiro cao mwa anthu;

27. Ndikadapanda kuopa mkwiyo wapamdani,Angayese molakwa outsana nao,Anganene, Lakwezeka dzanja lathu,Ndipo Yehova sanacita ici conse.

28. Popeza iwo ndiwo mtundu wa anthu wosowa uphungu konse,Ndipo alibe cidziwitso.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 32