23. Ndidzawaunjikira zoipa;Ndidzawathera nubvi yanga.
24. Adzaonda nayo njalaAdzanyekeka ndi makala a moto, cionongeko cowawa;Ndipo ndidzawatumizira mana a zirombo,Ndi ululu wa zokwawa m'pfumbi.
25. Pabwalo lupanga lidzalanda,Ndi m'zipinda mantha;Lidzaononga mnyamata ndi namwali,Woyamwa pamodzi ndi munthu waimvi.
26. Ndinati, Ndikadawauzira ndithu,Ndikadafafaniza cikumbukiro cao mwa anthu;
27. Ndikadapanda kuopa mkwiyo wapamdani,Angayese molakwa outsana nao,Anganene, Lakwezeka dzanja lathu,Ndipo Yehova sanacita ici conse.
28. Popeza iwo ndiwo mtundu wa anthu wosowa uphungu konse,Ndipo alibe cidziwitso.