18. Mwaleka Thanthwe limene linakubalani,Mwaiwala Mulungu amene anakulengani.
19. Ndipo Yehova anaciona, nawanyoza,Pakuipidwa nao ana ace amuna, ndi akazi.
20. Ndipo iye anati, Ndidzawabisira nkhope yanga,Ndidzaona kutsiriza kwao;Popeza iwo ndiwo mbadwo wopulukira,Ana osakhulupirika iwo.
21. Anautsa nsanje yanga ndi cinthu cosati Mulungu;Anautsa mkwiyo wanga om zopanda pace zao.Ndidzautsa nsanje yao ndi iwo osakhala mtundu wa anthu;Ndidzautsa mkwiyo wao ndi mtundu wa anthu opusa.
22. Pakuti wayaka moto mu mkwiyo wanga,Utentha kumanda kunsiUkutha dziko lapansi ndi zipatso zaceNuyatsa maziko a mapiri,
23. Ndidzawaunjikira zoipa;Ndidzawathera nubvi yanga.
24. Adzaonda nayo njalaAdzanyekeka ndi makala a moto, cionongeko cowawa;Ndipo ndidzawatumizira mana a zirombo,Ndi ululu wa zokwawa m'pfumbi.
25. Pabwalo lupanga lidzalanda,Ndi m'zipinda mantha;Lidzaononga mnyamata ndi namwali,Woyamwa pamodzi ndi munthu waimvi.