1. Kumwamba kuchere khutu, ndipo ndidzanena;Ndi dziko lapansi limve mau a m'kamwa mwanga;
2. Ciphunzitso canga cikhale ngati mvula;Maneno anga agwe ngati mame;Ngati mvula yowaza pamsipu,Ndi monga madontho a mvula pazitsamba.
3. Pakuti ndidzalalika dzina la Yehova;Nenani kuti Mulungu wathu ndi wamkulu.
4. Thanthwe, nchito yace ndi yangwiro;Pakuti njira zace zonse ndi ciweruzo;Mulungu wokhulupirika ndi wopanda cisalungamo;Iye ndiye wolungama ndi wolunjika,
5. Anamcitira zobvunda si ndiwo ana ace, cirema ncao;Iwo ndiwo mbadwo wopulukira ndi wokhotakhota.
6. Kodi mubwezera Yehova cotero,Anthu inu opusa ndi opanda nzeru?Kodi si ndiye Atate wanu, Mbuyewanu;Anakulengani, nakukhazikitsani?