Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 31:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Mose anamuka nanena mau awa kwa Israyeli wonse,

2. nati nao, Ndine munthu wa zaka zana ndi makumi awiri lero lino; sindikhozanso kuturuka ndi kulowa ndipo Yehova anati kwa ine, Sudzaoloka Yordano uyu.

3. Yehova Mulungu wanu ndiye adzaoloka pamaso panu, iye ndiye adzaononga amitundu awo pamaso panu, ndipo mudzawalandira. Yoswa ndiye adzakutsogolerani pooloka, monga ananena Yehova.

4. Ndipo Yehova adzawacitira monga anacitira Sihoni ndi Ogi, mafumu a Aamori, ndi dziko lao limene analiononga.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 31