Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 3:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Koma Yehova anakwiya ndi ine, cifukwa ca inu, sanandimvera ine; ndipo Yehova anati kwa ine, Cikukwanire, usaonjezenso kunena ndi Ine za cinthuci.

27. Kwera kumwamba ku Pisiga, nukweze maso ako kumadzulo, ndi kumpoto, ndi kumwela, ndi kum'mawa, nuyang'ane ndi maso ako; popeza sudzaoloka Yordano uyo.

28. Koma langiza Yoswa, dioloketu numlimbitse mtima, ndi kumkhwimitsa, pakuti adzaoloka pamaso pa anthu awa, nadzawalandiritsa dziko ulionali likhale lao lao.

29. Potero tinakhala m'cigwamo pandunji pa Beti Peori.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 3