Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 29:9-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Cifukwa cace sungani mau a cipangano ici ndi kuwacita, kuti mucite mwanzeru m'zonse muzicita.

10. Muimirira inu nonse lero lino pamaso pa Yehova Mulungu wanu; mafumu anu, mapfuko anu, akuru anu, ndi akapitao anu, amuna onse a Israyeli;

11. makanda anu, akazi anu, ndi mlendo wanu wakukhala pakati pa zigono zanu, kuyambira wotema nkhuni kufikira wotunga madzi;

12. kuti mulowe cipangano ca Yehova Mulungu wanu, ndi lumbiriro lace, limene Yehova Mulungu wanu acita ndi inu lero lino;

13. kuti adzikhazikire inu, mtundu wace wa anthu lero lino, ndi kuti akhale kwa inu Mulungu, monga ananena ndi inu, ndi monga analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isake, ndi Yakobo.

14. Koma sindicita cipangano ici ndi lumbiro ili ndi inu nokha;

15. komanso ndi iye wakuimirira pano nafe lero lino pamaso pa Yehova Mulungu wathu, ndiponso ndi iye wosakhala pano nafe lero lino.

16. Pakuti mudziwa cikhalidwe cathu m'dziko la Aigupto, ndi kuti tinapyola pakati pa amitundu amene munawapyola;

17. ndipo munapenya zonyansa zao, ndi mafano ao, mtengo ndi mwala, siliva ndi golidi, zokhala pakati pao;

18. kuti angakhale pakati pa inu mwamuna, kapena mkazi, kapena banja, kapena pfuko, mtima wao watembenuka kusiyana naye Yehova Mulungu wathu lero lino, kuti apite ndi kutumikira milungu ya amitundu aja; kuti ungakhale pakati pa inu muzu wakubala ndulu ndi cowawa.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 29