Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 27:11-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo Mose anauza anthu tsiku lomwelo, ndi kuti,

12. Aimirire awa pa phiri la Gerizimu kudalitsa anthu, mutaoloka Yordano: Simeoni ndi Levi, ndi Yuda, ndi Isakara, ndi Yosefe, ndi Benjamini.

13. Naimirire awa pa phiri la Ebala, kutemberera: Rubeni, Gadi, ndi Aseri, ndi Zebuloni, Dani, ndi Nafitali.

14. Ndipo ayankhe Alevi ndi kunena kwa amuna onse a Israyeli, ndi mau omveka.

15. Wotembereredwa munthu wakupanga fano losema kapena loyenga, lonyansidwa nalo Yehova, nchito ya manja a mmisiri, ndi kuliika m'malo a m'tseri. Ndipo anthu onse: ayankhe ndi kuti, Amen.

16. Wotembereredwa iye wakupeputsa atate wace kapena mai wace. Ndi anthu onse anene, Amen.

17. Wotembereredwa iye wakusendeza malire a mnansi wace. Ndi anthu onse anene, Amen.

18. Wotembereredwa wakusokeretsa wakhungu m'njira, Ndi anthu onse anene, Amen.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 27