Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 25:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. pamenepo muzidula dzanja lace; diso lanu lisamcitire cifundo.

13. Musamakhala nayo m'thumba mwanu miyala ya miyeso iwiri, waukuru ndi waung'ono.

14. Musamakhala nayo m'nyumba yanu miyeso ya efa yosiyana, waukuru ndi waung'ono.

15. Muzikhala nao mwala wa muyeso wofikira ndi woyenera; mukhale nao muyeso wa efa wofikira ndi woyenera; kuti masiku anu acuruke m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani.

16. Pakuti onse akucita zinthu izi, onse akucita cisalungamo, Yehova Mulungu wanu anyansidwa nao.

17. Kumbukilani cocitira inu Amaleki panjira, poturuka inu m'Aigupto;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 25