28. Munthu akapeza namwali wosadziwa mwamuna, ndiye wosapalidwa ubwenzi, oakamgwira nagona naye, napezedwa iwo,
29. pamenepo mwamuna amene anagona naye azipatsa atate wace wa namwaliyo masekeli makumi asanu a siliva, ndipo azikhala mkazi wace; popeza anamcepetsa; sakhoza kumcotsa masiku ace onse.
30. Munthu asatenge mkazi wa atate wace, kapena kubvula atate wace.