Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 22:27-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. pakuti anampeza kuthengo; namwali wopalidwa bwenziyo anapfuula, koma panalibe wompulumutsa.

28. Munthu akapeza namwali wosadziwa mwamuna, ndiye wosapalidwa ubwenzi, oakamgwira nagona naye, napezedwa iwo,

29. pamenepo mwamuna amene anagona naye azipatsa atate wace wa namwaliyo masekeli makumi asanu a siliva, ndipo azikhala mkazi wace; popeza anamcepetsa; sakhoza kumcotsa masiku ace onse.

30. Munthu asatenge mkazi wa atate wace, kapena kubvula atate wace.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 22