Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 21:21-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Pamenepo amuna onse a mudzi wace amponye miyala kuti afe; cotero mucotse coipaco pakati panu; ndipo Israyeli wonse adzamva, nadzaopa.

22. Munthu akakhala nalo cimo loyenera imfa, kuti amuphe, ndipo wampacika;

23. mtembo wace usakhale pamtengo usiku wonse, koma mumuike ndithu tsiku lomwelo; pakuti wopacikidwa pamtengo atembereredwa ndi Mulungu; kuti mungadetse dziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colowa canu.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 21