Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 21:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Munthu akakhala naye mwana wamwamuna wopulukira, ndi wopikisana naye, wosamvera mau a atate wace, kapena mau a mai wace, wosawamvera angakhale anamlanga;

19. azimgwira atate wace ndi mai wace, ndi kuturukira naye kwa akuru a mudzi wace, ndi ku cipata ca malo ace;

20. ndipo anene kwa akulu a mudzi wace, Mwana wathu wamwamuna uyu ngwopulukira ndi wopikisana nafe, wosamvera mau athu, ndiye womwazamwaza, ndi woledzera.

21. Pamenepo amuna onse a mudzi wace amponye miyala kuti afe; cotero mucotse coipaco pakati panu; ndipo Israyeli wonse adzamva, nadzaopa.

22. Munthu akakhala nalo cimo loyenera imfa, kuti amuphe, ndipo wampacika;

23. mtembo wace usakhale pamtengo usiku wonse, koma mumuike ndithu tsiku lomwelo; pakuti wopacikidwa pamtengo atembereredwa ndi Mulungu; kuti mungadetse dziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colowa canu.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 21