Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 20:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Koma ukapanda kucita zamtendere ndi inu, koma kucita nkhondo nanu, pamenepo uumangire tsasa.

13. Ndipo pamene Yehova Mulungu wanu aupereka m'dzanja lanu, mukanthe amuna ace onse ndi lupanga lakuthwa.

14. Koma akazi ndi ana ndi ng'ombe ndi zonse ziti m'mudzimo, zankhondo zace zonse, mudzifunkhire nokha; ndipo mudye zankhondo za adani anu, zimene Yehova Mulungu wanu anakupatsani.

15. Muzitero nayo midzi yonse yokhala kutaritari ndi inu, yosakhala midzi ya amitundu awa.

16. Koma za midzi ya amitundu awa, imene Yehova Mulungu wanu akupatsani, ikhale colowa canu, musasiyepo camoyo ciri conse cakupuma;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 20