Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 19:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. ndipo oweruza afunsitse bwino; ndipo taonani, mboniyo ikakhala mboni yonama, yomnamizira mbale wace;

19. mumcitire monga iye anayesa kumcitira mbale wace; motero mucotse coipaco pakati panu.

20. Ndipo otsalawo adzamva, nadzaopa, ndi kusacitanso monga coipaco pakati panu.

21. Ndipo diso lanu lisacite cifundo, moyo kulipa moyo, diso kulipa diso, dzino kulipa dzino, dzanja kulipa dzanja, phazi kulipa phazi.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 19