Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 18:8-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Cakudya cao cizifanana, osawerengapo zolowa zace zogulitsa.

9. Mutakalowa m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, musamaphunzira kucita mongamwa zonyansa za amitundu aja.

10. Asapezeke mwa inu munthu wakupitiriza mwana wace wamwamuna kapena mwana wace wamkazi ku mota wa ula, wosamalira mitambo, kapena wosamalira kulira kwa mbalame, kapena wanyanga.

11. Kapena wotsirika, kapena wobwebweta, kapena wopenduza, kapena wofunsira akufa.

12. Popeza ali yense wakucita izi Yehova anyansidwa naye; ndipo cifukwa ca zonyansa izi Yehova Mulungu wanu awapitikitsa pamaso panu.

13. Mukhale angwiro ndi Yehova Mulungu wanu.

14. Pakuti amitundu awa amene mudzawalandira, amamvera iwo akuyesa mitambo, ndi a ula; koma inu, Yehova Mulungu wanu sakulolani kucita cotero.

15. Yehova Mulungu wanu adzakuukitsirani mneneri wa pakati panu, wa abale anu, wonga ine; muzimvera iye;

16. monga mwa zonse munafunsa Yehova Mulungu wanu m'Horebe, tsiku lakusonkhana lija, ndi kuti, Tisamvenso mau a Yehova Mulungu wathu, ndipo tisaonenso mota waukuru uwu, kuti tingafe.

17. Ndipo Yehova anati kwa ine, Cokoma ananenaci.

18. Ndidzawaukitsira mneneri wa pakati pa abale ao, wonga iwe; ndipo ndidzampatsa mau anga m'kamwa mwace, ndipo adzanena nao zonse ndimuuzazi.

19. Ndipo kudzakhala kuti munthu wosamvera mau anga amene amanena m'dzina langa, ndidzamfunsa.

20. Koma mneneri wakucita modzikuza ndi kunena mau m'dzina langa, amene sindinamlamulira anene, kapena kunena m'dzina la milungu yina, mneneri ameneyo afe.

21. Ndipo mukati m'mtima mwanu, Tidzazindikira bwanji mau amene Yehova sananena?

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 18