Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 18:20-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Koma mneneri wakucita modzikuza ndi kunena mau m'dzina langa, amene sindinamlamulira anene, kapena kunena m'dzina la milungu yina, mneneri ameneyo afe.

21. Ndipo mukati m'mtima mwanu, Tidzazindikira bwanji mau amene Yehova sananena?

22. Mneneri akanena m'dzina la Yehova, koma mau adanenawa sacitika, nisafika, ndiwo mau Yehova sanawanena; mneneriyo ananena modzikuza, musamuopa iye.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 18