Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 14:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. ngondo, ndi nswala ndi mphoyo, ndi mphalapala, ndi ngoma, ndi nyumbu, ndi mbalale.

6. Ndipo nyama iri yonse yogawanika ciboda, nikhala yogawanikadi ciboda, nibzikula, imeneyo muyenera kudya.

7. Koma izi zokha simuyenera kuzidya mwa zobzikulazo, kapena zogawanika ciboda: ngamila, ndi ka'ulu, ndi mbira, popezazibzikula, komazosagawanika ciboda, muziyese zodetsa;

8. ndi nkhumba, popeza igawanika ciboda koma yosabzikula, muiyese yodetsa; musamadya nyama yao, musamakhudza mitembo yao.

9. Mwa zonse ziri m'madzi muyenera kumadya izi: ziri zonse ziri nazo zipsepse ndi mamba, zimenezi muyenera kumadya;

10. koma ziri zonse zopanda zipsepse kapena mamba musamadya; muziyese zonyansa.

11. Mbalame zosadetsazonse muyenera kumadya.

12. Koma izi ndi zimene simuyenera kumadya: mphungu, ndi nkhwazi, ndi cikambi,

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 14