Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 10:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Popeza Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu wa milungu, ndi Mbuye ya ambuye; Mulungu wamkuru, wamphamvu, ndi woopsa, wosasamalira nkhope za anthu, kapena kulandira cokometsera mlandu.

18. Aweruzira ana amasiye ndi mkazi wamasiye; ndipo akonda mlendo, ndi kumpatsa cakudya ndi cobvala.

19. M'mwemo mukondane naye mlendo; popeza munali alendo m'dziko la Aigupto.

20. Muziopa Yehova Mulungu wanu; mumtumikire Iyeyo; mummamatire iye, ndi kulumbira pa dzina lace.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 10