Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 10:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Masiku aja Yehova anati kwa ine, Dzisemere magome awiri amiyala onga oyamba aja, nukwere kuno kwa Ine m'phiriumu, nudzipangire likasa lamtengo.

2. Ndipo ndidzalembera pa magomewo mauwo anali pa magome oyamba aja amene unawaswa, ndipo uwaike m'likasamo.

3. Potero ndinapanga likasa la mtengo wasitimu, ndinasemanso magome awiri amiyala onga oyamba aja, ndi kukwera m'phirimo, magome awiri ali m'manja mwanga.

4. Ndipo analembera pamagome, monga mwa malembedwe oyamba, mau khumiwo, amene Yehova adanena ndi inu m'phirimo, ali pakati pa moto, tsiku la kusonkhanako; ndipo Yehova anandipatsa awa.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 10