44. Ndipo Aamori, akukhala m'mapiri muja, anaturuka kukomana ndi inu, nakupitikitsani, monga zimacita njuci, nakukanthani m'Seiri, kufikira ku Horima.
45. Ndipo munabwerera ndi kulira pamaso pa Yehova; koma Yehova sanamvera mau anu, kapena kukucherani khutu.
46. Potero munakhala m'Kadesi masiku ambiri, monga mwa masiku munakhalako.