Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 1:26-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Koma simunafuna kukwerako, ndipo munapikisana nao mau a Yehova Mulungu wanu.

27. Ndipo munadandaula m'mahema mwanu, ndi kuti, Popeza anatida Yehova, iye anatiturutsa m'dziko la Aigupto, kutipereka m'manja mwa Aamori, ationonge.

28. Tikwere kuti? abale athu atimyukitsa mitima yathu, ndi kuti, Anthuwo ndiwo akulu ndi atali akuposa ife; midzi ndi yaikulu ndi ya malinga ofikira m'mwamba: tinaonakonso ana a Anaki.

29. Pamenepo ndinati kwa inu, Musamaopsedwa, musamacita mantha nao.

30. Yehova Mulungu wanu wakutsogolera inu, iye adzathirira inu nkhondo, monga mwa zonse anakucitirani m'Aigupto pamaso panu;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 1