Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 1:23-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo cinandikomera cinthu ici; ndipo ndinatenga amuna khumi ndi awiri ainu, pfuko limodzi mwamuna mmodzi;

24. amenewa anatembenuka nakwera kumapiri nalowa ku cigwa ca Esikolo, nacizonda.

25. Ndipo anatengako zipatso za dzikoli m'manja mwao, natsikira nazo kwa ife, natibwezera mau ndi kuti, Dzikoli Yehova Mulungu wathu atipatsa ndi labwino.

26. Koma simunafuna kukwerako, ndipo munapikisana nao mau a Yehova Mulungu wanu.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 1