1. Ambuye Yehova anandionetsa cotere; ndipo taonani, anaumba dzombe, poyamba kuphuka kwa maudzu a cibwereza; ndipo taonani, ndico cibwereza atawasengera mfumu.
2. Ndipo kunacitika m'mene lidatha kudya msipu wa dziko, ndinati, Ambuye Yehova, khululukiranitu Yakobo; adzakhala ciriri bwanji? popeza ndiye wamng'ono.
3. Ndipo Yehova anacileka. Sicidzacitika, ati Yehova.